RUMPHI (MaraPost) –Mkulu wojijiduka mchipani cholamula cha Peoples Party Ken Msonda lolemba lapitali adakalembetsa mkaundula wa mavoti kuti adzathe kuvota mchisankho chimene chilli nkubwela mu mchaka cha 2014.
Bambo Msonda adalengeza kuti iwo akufuna kudzayimira chipani cha PP ngati phungu ku dera la kwao ku Rumphi.
Mchinthuzichi, bambo Msonda akuoneka pa line kudikilira kuti alembetse kwawo ku Rumphi.
Ngati inu simudalembetse ndipo muli kudera limene kalembera ali mkati, chonde kalembetseni kuti mudzakhale nawo mwayi osankha munthu wa ku mtima kwanu.